< Masalimo 65 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
A ti, ó Deus, espera o louvor em Sião, e a ti se pagará o voto.
2 Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
Ó tu que ouves as orações, a ti virá toda a carne.
3 Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
Prevalecem as iniquidades contra mim; porém tu expias as nossas transgressões.
4 Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
Bemaventurado aquelle a quem tu escolhes, e fazes chegar a ti, para que habite em teus atrios: nós seremos fartos da bondade da tua casa e do teu sancto templo.
5 Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
Pelas coisas tremendas em justiça nos responderás, ó Deus da nossa salvação; tu és a esperança de todas as extremidades da terra, e d'aquelles que estão longe sobre o mar.
6 amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
O que pela sua força consolida os montes, cingido de fortaleza:
7 Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
O que applaca o ruido dos mares, o ruido das suas ondas, e o tumulto das gentes.
8 Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
E os que habitam nos fins da terra temem os teus signaes; tu fazes alegres as saidas da manhã e da tarde.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
Tu visitas a terra, e a refrescas; tu a enriqueces grandemente com o rio de Deus, que está cheio d'agua; tu lhe preparas o trigo, quando assim a tens preparada.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
Enches d'agua os seus regos, fazendo-a descer em suas margens: tu a amoleces com a muita chuva: abençoas as suas novidades.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
Coroas o anno da tua bondade, e as tuas veredas distillam gordura.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
Distillam sobre os pastos do deserto, e os outeiros os cingem de alegria.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
Os campos se vestem de rebanhos, e os valles se cobrem de trigo: elles se regozijam e cantam.

< Masalimo 65 >