< Masalimo 65 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
Psalmus David, in finem. Canticum Hieremiae, et Ezechielis ex populo transmigrationis, cum inciperent exire. Te decet hymnus Deus in Sion: et tibi reddetur votum in Ierusalem.
2 Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
Exaudi orationem meam: ad te omnis caro veniet.
3 Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
Verba iniquorum praevaluerunt super nos: et impietatibus nostris tu propitiaberis.
4 Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
Beatus, quem elegisti, et assumpsisti: inhabitabit in atriis tuis. Replebimur in bonis domus tuae: sanctum est templum tuum,
5 Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
mirabile in aequitate. Exaudi nos Deus salutaris noster, spes omnium finium terrae, et in mari longe.
6 amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
Praeparans montes in virtute tua, accinctus potentia:
7 Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
qui conturbas profundum maris sonum fluctuum eius. Turbabuntur gentes,
8 Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
et timebunt qui habitant terminos a signis tuis: exitus matutini et vespere delectabis.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
Visitasti terram et inebriasti eam: multiplicasti locupletare eam. Flumen Dei repletum est aquis, parasti cibum illorum: quoniam ita est praeparatio eius.
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
Rivos eius inebria, multiplica genimina eius: in stillicidiis eius laetabitur germinans.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
Benedices coronae anni benignitatis tuae: et campi tui replebuntur ubertate.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
Pinguescent speciosa deserti: et exultatione colles accingentur.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
Induti sunt arietes ovium, et valles abundabunt frumento: clamabunt, etenim hymnum dicent.

< Masalimo 65 >