< Masalimo 65 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
A karmesternek. Zsoltár Dávidtól. Ének. Hozzád illő a dicsérő dal, oh Isten, Cziónban, és neked fizettessék a fogadalom!
2 Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
Meghallója az imának, te eléd járul minden halandó.
3 Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
A bűnök dolgai elhatalmasodtak rajtam; bűntetteinket, te bocsásd meg azokat!
4 Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
Boldog, a kit megválasztasz és közeledni engedsz, hogy lakozzék udvaraidban! Hadd lakjunk jól javával házadnak, szent templomodnak!
5 Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
Félelmetes dolgokkal igazságban hallgass meg minket, üdvünk Istene, bizodalma mind a föld végeinek és a távoli tengernek;
6 amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
a ki megszilárdítja a hegyeket erejével, felövezkedve hatalommal,
7 Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
lecsillapítja tengerek zajongását, hullámaik zajongását és nemzetek zúgását.
8 Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
S megfélemedtek a végek lakói jeleidtől, reggel és est keletjeit megujjongtatod.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
Gondoltál tt földre és megáztattad, bőven meggazdagítod, Isten patakjából, mely vizzel teli; elkészíted gabnájukat, mert így készíted őt elő:
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
barázdáit öntözve, lelapítva göröngyeit, záporesővel megpuhítod, megáldod növényzetét.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
Megkoronázod az esztendőt jóságoddal, és ösvényeid zsiradéktól csurognak.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
Csurognak a puszta tanyái s ujjongással övezkednek a halmok;
13 Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
öltöttek juhokat a rétek és a völgyek gabonába burkolóznak, riadoznak meg énekelnek!

< Masalimo 65 >