< Masalimo 65 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
Au maître-chantre. — Psaume de David. — Cantique. Une paisible confiance en toi, ô Dieu, Voilà ta louange en Sion; C'est pour ta gloire Que nous voulons nous acquitter de nos voeux.
2 Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
toi qui entends la prière. Toutes les créatures viendront à toi!
3 Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
Le poids des iniquités m'accable; Mais toi, tu pardonnes nos transgressions.
4 Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
Heureux celui que tu choisis et que tu prends avec toi, Pour le faire habiter dans tes parvis! Nous nous rassasierons des biens de ta maison. Des biens de ton saint temple!
5 Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
Tu nous réponds par les oeuvres redoutables de ta justice, Dieu de notre salut, Espoir des extrémités de la terre et des mers lointaines!
6 amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
C'est Dieu qui soutient les montagnes par sa force; Il est ceint de puissance.
7 Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
Il apaise le grondement des mers, Le grondement de leurs flots, Et le tumulte des peuples.
8 Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
Ceux qui habitent aux extrémités de la terre Sont remplis de crainte, A la vue de tes prodiges. Tu fais tressaillir d'allégresse et le Levant et le Couchant.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
Tu visites la terre, tu l'arroses, Tu l'enrichis abondamment. Les ruisseaux de Dieu sont pleins d'eau. Tu prépares le blé lorsque, pour fertiliser la terre,
10 Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
Tu en abreuves les sillons, tu en aplanis les mottes. Tu la détrempes par les pluies et tu bénis ses fruits.
11 Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
Tu couronnes l'année de tes biens, Et, sur sa route, ton char répand l'abondance.
12 Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
Les pâturages du désert sont abondamment arrosés, Et les collines ont la joie pour parure.
13 Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
Les campagnes se revêtent de troupeaux, Et les vallées se couvrent de froment: Partout des cris et des chants d'allégresse!

< Masalimo 65 >