< Masalimo 64 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Poslušaj moj glas, oh Bog, v moji molitvi, varuj moje življenje strahu pred sovražnikom.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Skrij me pred skrivnim načrtom hudobnih, pred vstajo delavcev krivičnosti,
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
ki brusijo svoj jezik kakor meč in upogibajo svoje loke, da bi streljali svoje puščice, celó grenke besede,
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
da bi lahko na skrivnem streljali na popolnega. Nenadoma streljajo nanj in se ne bojijo.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
Med seboj se hrabrijo v zli zadevi. Na skrivaj se posvetujejo o nastavljanju zank; pravijo: »Kdo jih bo videl?«
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
Preiskujejo krivičnosti, dovršijo marljivo iskanje. Notranja misel vsakogar izmed njih in srce, oboje je globoko.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
Toda Bog bo nanje streljal s puščico, nenadoma bodo ranjeni.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
Tako bodo dosegli, da bo njihov lastni jezik padel nanje. Vsi, ki jih vidijo, bodo zbežali stran.
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
Vsi ljudje se bodo bali in bodo oznanjali Božje delo, kajti o njegovem dejanju bodo modro preudarjali.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
Pravični bodo veseli v Gospodu in bodo zaupali vanj in vsi iskreni v srcu bodo ponosni.

< Masalimo 64 >