< Masalimo 64 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Salmo de Davi, para o regente: Ouve, Deus, minha voz, em minha meditação [de súplica]; guarda minha vida do terror do inimigo.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Esconde-me do grupo dos malignos, e do ajuntamento dos praticantes de maldade,
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Que afiam sua língua como [se fosse] espada; e armaram palavras amargas [como se fossem] flechas.
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
Para atirarem no inocente às escondidas; disparam apressadamente contra ele, e não têm medo.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
Eles são ousados para [fazerem] coisas más, comentam sobre como esconder armadilhas, [e] dizem: Quem as verá?
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
Eles buscam por perversidades; procuram tudo o que pode ser procurado, até o interior de [cada] homem, e as profundezas do coração.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
Mas Deus os atingirá com flecha de repente; e [logo] serão feridos.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
E a língua deles fará com que tropecem em si mesmos; todo aquele que olhar para eles se afastará.
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
E todos os homens terão medo, e anunciarão a obra de Deus, e observarão cuidadosamente o que ele fez.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
O justo se alegará no SENHOR, e confiará nele; e todos os corretos de coração [o] glorificarão.

< Masalimo 64 >