< Masalimo 64 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
למנצח מזמור לדוד ב שמע-אלהים קולי בשיחי מפחד אויב תצר חיי
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
תסתירני מסוד מרעים מרגשת פעלי און
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
אשר שננו כחרב לשונם דרכו חצם דבר מר
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
לירת במסתרים תם פתאם ירהו ולא ייראו
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
יחזקו-למו דבר רע-- יספרו לטמון מוקשים אמרו מי יראה-למו
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
יחפשו עולת-- תמנו חפש מחפש וקרב איש ולב עמק
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
וירם אלהים חץ פתאום--היו מכותם
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
ויכשילוהו עלימו לשונם יתנדדו כל-ראה בם
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
וייראו כל-אדם ויגידו פעל אלהים ומעשהו השכילו
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
ישמח צדיק ביהוה וחסה בו ויתהללו כל-ישרי-לב

< Masalimo 64 >