< Masalimo 64 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
To the chief Musician, a Psalm of David. Hear my voice, O God, in my prayer: preserve my life from fear of the enemy.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Hide me from the secret counsel of the wicked; from the insurrection of the workers of iniquity:
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Who whet their tongue like a sword, [and] bend [their bows to shoot] their arrows, [even] bitter words:
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
That they may shoot in secret at the perfect: suddenly do they shoot at him, and fear not.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
They encourage themselves [in] an evil matter: they commune of laying snares privily; they say, Who will see them?
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
They search out iniquities; they accomplish a diligent search: both the inward [thought] of every one [of them], and the heart, [is] deep.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
But God shall shoot at them [with] an arrow; suddenly shall they be wounded.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
So they shall make their own tongue to fall upon themselves: all that see them shall flee away.
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
And all men shall fear, and shall declare the work of God; for they shall wisely consider of his doing.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
The righteous shall be glad in the LORD, and shall trust in him; and all the upright in heart shall glory.