< Masalimo 64 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
To the Chief Musician. A Melody of David. Hear, O God, my voice when I complain, From dread peril by the foe, wilt thou guard my life.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Wilt thou hide me, From the conclave of evil-doers, From the crowd of workers of iniquity.
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Who have sharpened, like a sword, their tongue, Have made ready their arrow—a bitter word;
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
To shoot, in secret places, at the blameless one, Suddenly they shoot at him, and fear not.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
They strengthen for them a wicked word, They talk of hiding snares, They have said, Who can see them?
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
They devise perverse things, They have completed the device well devised, Both the intent of each one, and the mind, are unsearchable.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
Once let God have shot at them an arrow, Suddenly have appeared their own wounds!
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
When they were to have ruined another, their tongue smote themselves, All who observe them take flight.
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
Therefore have all men feared, —And have told the doing of God, And, his work, have considered.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
The righteous man shall rejoice in Yahweh, and seek refuge in him, Then shall glory—all who are upright in heart.

< Masalimo 64 >