< Masalimo 64 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
To the chief Musician. A Psalm of David. Hear, O God, my voice in my plaint; preserve my life from fear of the enemy:
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Hide me from the secret counsel of evil-doers, from the tumultuous crowd of the workers of iniquity,
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
Who have sharpened their tongue like a sword, [and] have aimed their arrow, a bitter word;
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
That they may shoot in secret at the perfect: suddenly do they shoot at him, and fear not.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
They encourage themselves in an evil matter, they concert to hide snares; they say, Who will see them?
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
They devise iniquities: We have it ready, the plan is diligently sought out. And each one's inward [thought] and heart is deep.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
But God will shoot an arrow at them: suddenly are they wounded;
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
By their own tongue they are made to fall over one another: all that see them shall flee away.
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
And all men shall fear, and shall declare God's doing; and they shall wisely consider his work.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
The righteous shall rejoice in Jehovah, and trust in him; and all the upright in heart shall glory.

< Masalimo 64 >