< Masalimo 64 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Zborovođi. Psalam. Davidov. Poslušaj, Bože, moje žalbe glas; od strašna dušmanina život mi čuvaj!
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Štiti me od mnoštva opakih, sakrij od bjesnila zlotvora
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
koji bruse jezike k'o mačeve, otrovne riječi izbacuju kao strijele,
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
da iz potaje rane nedužna, da ga rane iznenada ne bojeć' se ničega.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
Spremni su na djelo pakosno, snuju kako će kradom zamke staviti i govore: “Tko će nas vidjeti?”
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
Snuju zlodjela, smišljene osnove kriju: pamet i srce čovječje bezdan su duboki.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
No Bog ih ranjava strijelom, odjednom ih rane prekriju.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
Vlastiti jezik propast im donosi, kimaju glavom oni što ih vide:
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
svi se boje, Božje djelo slave i misle o onom što on učini.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
Pravednik se raduje u Jahvi, njemu se utječe, i kliču svim srcem čestiti.