< Masalimo 63 >

1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
Псалом Давидів, коли він був у пустелі Юдейській. Боже, Ти – мій Бог, Тебе я пристрасно шукаю. Душа моя спрагла Тебе, тіло моє тужить за Тобою у землі висохлій і виснаженій, де немає води.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Так я споглядав Тебе у святилищі, щоб побачити могутність Твою і славу.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Бо милість Твоя краща від [самого] життя, [тому] вуста мої хвалитимуть Тебе.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Я благословлятиму Тебе, поки житиму, в ім’я Твоє піднесу мої руки.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
Неначе лоєм і олією, насичується душа моя, і вуста мої радісно прославляють Тебе,
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
коли я згадую Тебе на моєму ложі, у нічні години роздумую про Тебе.
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Бо Ти був мені допомогою, і в тіні Твоїх крил я радітиму.
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
Прилинула до Тебе душа моя, правиця ж Твоя підтримує мене.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
А ті, хто прагне загибелі для душі моєї, нехай зійдуть у глибини землі.
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
Нехай віддані мечу, вони стануть здобиччю лисиць.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
Цар же нехай радіє Богом, нехай прославляють Його всі, хто Ним присягає, та замовкнуть вуста тих, хто промовляє неправду.

< Masalimo 63 >