< Masalimo 63 >
1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
psalmus David cum esset in deserto Iudaeae Deus Deus meus ad te de luce vigilo sitivit in te anima mea quam multipliciter tibi caro mea
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
in terra deserta et invia et inaquosa sic in sancto apparui tibi ut viderem virtutem tuam et gloriam tuam
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
quoniam melior est misericordia tua super vitas labia mea laudabunt te
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
sic benedicam te in vita mea in nomine tuo levabo manus meas
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
sicut adipe et pinguidine repleatur anima mea et labia exultationis laudabit os meum
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
si memor fui tui super stratum meum in matutinis meditabar in te
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
quia fuisti adiutor meus et in velamento alarum tuarum exultabo
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
adhesit anima mea post te me suscepit dextera tua
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
ipsi vero in vanum quaesierunt animam meam introibunt in inferiora terrae
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
tradentur in manus gladii partes vulpium erunt
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
rex vero laetabitur in Deo laudabitur omnis qui iurat in eo quia obstructum est os loquentium iniqua