< Masalimo 63 >

1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
Psalmus David, Cum esset in deserto Idumaeae. Deus Deus meus ad te de luce vigilo. Sitivit in te anima mea, quam multipliciter tibi caro mea.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
In terra deserta, et invia, et inaquosa: sic in sancto apparui tibi, ut viderem virtutem tuam, et gloriam tuam.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Quoniam melior est misericordia tua super vitas: labia mea laudabunt te.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Sic benedicam te in vita mea: et in nomine tuo levabo manus meas.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
Sicut adipe et pinguedine repleatur anima mea: et labiis exultationis laudabit os meum.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Sic memor fui tui super stratum meum, in matutinis meditabor in te:
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
quia fuisti adiutor meus. Et in velamento alarum tuarum exultabo,
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
adhaesit anima mea post te: me suscepit dextera tua.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
Ipsi vero in vanum quaesierunt animam meam, introibunt in inferiora terrae:
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
tradentur in manus gladii, partes vulpium erunt.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
Rex vero laetabitur in Deo, laudabuntur omnes qui iurant in eo: quia obstructum est os loquentium iniqua.

< Masalimo 63 >