< Masalimo 63 >

1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
Psaume de David. Lorsqu’il était dans le désert de Juda. O Dieu! Tu es mon Dieu, je te cherche; Mon âme a soif de toi, mon corps soupire après toi, Dans une terre aride, desséchée, sans eau.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Ainsi je te contemple dans le sanctuaire, Pour voir ta puissance et ta gloire.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Car ta bonté vaut mieux que la vie: Mes lèvres célèbrent tes louanges.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Je te bénirai donc toute ma vie, J’élèverai mes mains en ton nom.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
Mon âme sera rassasiée comme de mets gras et succulents, Et, avec des cris de joie sur les lèvres, ma bouche te célébrera.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Lorsque je pense à toi sur ma couche, Je médite sur toi pendant les veilles de la nuit.
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Car tu es mon secours, Et je suis dans l’allégresse à l’ombre de tes ailes.
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
Mon âme est attachée à toi; Ta droite me soutient.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
Mais ceux qui cherchent à m’ôter la vie Iront dans les profondeurs de la terre;
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
Ils seront livrés au glaive, Ils seront la proie des chacals.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
Et le roi se réjouira en Dieu; Quiconque jure par lui s’en glorifiera, Car la bouche des menteurs sera fermée.

< Masalimo 63 >