< Masalimo 63 >

1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
Psaume de David; quand il était dans le désert de Juda. Ô Dieu! tu es mon Dieu; je te cherche au point du jour; mon âme a soif de toi, ma chair languit après toi, dans une terre aride et altérée, sans eau,
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Pour voir ta force et ta gloire, comme je t’ai contemplé dans le lieu saint.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Car ta bonté est meilleure que la vie; mes lèvres te loueront.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Ainsi je te bénirai durant ma vie, j’élèverai mes mains en ton nom.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
Mon âme est rassasiée comme de moelle et de graisse, et ma bouche [te] louera avec des lèvres qui chantent de joie.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Quand je me souviens de toi sur mon lit, je médite de toi durant les veilles de la nuit;
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Car tu as été mon secours, et à l’ombre de tes ailes je chanterai de joie.
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
Mon âme s’attache à toi pour te suivre, ta droite me soutient.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
Mais ceux qui cherchent ma vie pour sa ruine entreront dans les parties inférieures de la terre;
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
On les livrera à la puissance de l’épée, ils seront la portion des renards.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
Mais le roi se réjouira en Dieu, [et] quiconque jure par lui se glorifiera; car la bouche de ceux qui parlent faussement sera fermée.

< Masalimo 63 >