< Masalimo 63 >

1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
God, you are the God whom I [worship]. I greatly desire to be with you like [SIL] a person in a dry hot desert greatly desires [some cool water].
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
So, I want to see you in your temple; I want to see that you are great and glorious.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Your constantly loving [me] is (worth more/more precious) than [my] life, so I [MTY] will [always] praise you.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
I will praise you all the time that I live; I will lift up my hands to you while I pray.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
[Knowing you satisfies me more than] [IDM, MET] my eating a very big feast, [so] I will praise you while I sing [MTY] joyful songs.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
While I lie on my bed, I think about you. I think/meditate about you all during the night,
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
because you have always helped me, and I sing joyfully knowing that I am protected by you [as a little bird is protected] under [its mother’s] wings [MET].
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
I cling to you; and with your hand/power you protect me.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
But those who are trying to kill me will [die and] descend into the place of the dead;
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
they will be killed in battles [MTY] and their [corpses] will be eaten by jackals/wild dogs.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
But I, the king [of Israel], will rejoice in what God has done; and all those who revere and trust God will praise him, but he will not allow liars to say anything.

< Masalimo 63 >