< Masalimo 63 >
1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
A Psalme of David. When he was in the wildernesse of Judah. O God, thou art my God, earely will I seeke thee: my soule thirsteth for thee: my flesh longeth greatly after thee in a barren and drye land without water.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
Thus I beholde thee as in the Sanctuarie, when I beholde thy power and thy glorie.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
For thy louing kindnesse is better then life: therefore my lippes shall prayse thee.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Thus will I magnifie thee all my life, and lift vp mine hands in thy name.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
My soule shalbe satisfied, as with marowe and fatnesse, and my mouth shall praise thee with ioyfull lippes,
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
When I remember thee on my bedde, and when I thinke vpon thee in the night watches.
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Because thou hast bene mine helper, therefore vnder the shadow of thy wings wil I reioyce.
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
My soule cleaueth vnto thee: for thy right hand vpholdeth me.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
Therefore they that seeke my soule to destroy it, they shall goe into the lowest partes of the earth.
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
They shall cast him downe with the edge of the sword, and they shall be a portion for foxes.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
But the King shall reioyce in God, and all that sweare by him shall reioyce in him: for the mouth of them that speake lyes, shall be stopped.