< Masalimo 63 >
1 Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
Psalam. Davidov. Dok David bijaše u Judejskoj pustinji. O Bože, ti si Bog moj: gorljivo tebe tražim; tebe žeđa duša moja, tebe želi tijelo moje, kao zemlja suha, žedna, bezvodna.
2 Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
U Svetištu sam tebe motrio gledajuć' ti moć i slavu.
3 Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
Ljubav je tvoja bolja od života, moje će te usne slavit'.
4 Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
Tako ću te slavit' za života, u tvoje ću ime ruke dizati.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
Duša će mi biti kao sala i mrsa sita, hvalit ću te kliktavim ustima.
6 Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
Na postelji se tebe spominjem, u bdjenjima noćnim mislim na tebe.
7 Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
Ti postade meni pomoć, kličem u sjeni krila tvojih.
8 Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
Duša se moja k tebi privija, desnica me tvoja drži.
9 Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
Oni što dušu u propast guraju neka siđu u dubinu zemlje,
10 Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
nek' vlasti mača predani budu, nek' postanu plijen šakalima.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.
A kralj će se radovat' u Bogu, slavit će se tko se kune njime, jer će lašcima biti začepljena usta.