< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
В конец, о Идифуме, псалом Давиду. Не Богу ли повинется душа моя? От Того бо спасение мое.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Ибо Той Бог мой и спас мой, заступник мой: не подвижуся наипаче.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Доколе належите на человека? Убиваете вси вы, яко стене преклонене и оплоту возриновену.
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Обаче цену мою совещаша отринути, текоша в жажди: усты своими благословляху, и сердцем своим кленяху.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Обаче Богови повинися, душе моя: яко от Того терпение мое.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Ибо Той Бог мой и спас мой, заступник мой: не преселюся.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
О Бозе спасение мое и слава моя: Бог помощи моея, и упование мое на Бога.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Уповайте на Него, весь сонм людий: излияйте пред Ним сердца ваша, яко Бог помощник наш.
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Обаче суетни сынове человечестии, лживи сынове человечестии в мерилех еже неправдовати: тии от суеты вкупе.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Не уповайте на неправду, и на восхищение не желайте: богатство аще течет, не прилагайте сердца.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Единою глагола Бог, двоя сия слышах, зане держава Божия,
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
и Твоя, Господи, милость: яко Ты воздаси комуждо по делом его.

< Masalimo 62 >