< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Да, нумай ын Думнезеу ми се ынкреде суфлетул; де ла Ел ымь вине ажуторул.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Да, Ел есте Стынка ши Ажуторул меу, Турнул меу де скэпаре; ничдекум ну мэ вой клэтина.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Пынэ кынд вэ вець нэпусти асупра унуй ом, пынэ кынд вець кэута ку тоций сэ-л доборыць ка пе ун зид гата сэ кадэ, ка пе ун гард гата сэ се сурпе?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Да, ей пун ла кале сэ-л добоаре дин ынэлцимя луй: ле плаче минчуна; ку гура бинекувынтязэ, дар ку инима блестемэ.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Да, суфлете, ынкреде-те ын Думнезеу, кэч де ла Ел ымь вине нэдеждя!
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Да, Ел есте Стынка ши Ажуторул меу, Турнул меу де скэпаре: ничдекум ну мэ вой клэтина.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Пе Думнезеу се ынтемеязэ ажуторул ши слава мя; ын Думнезеу есте стынка путерий меле, локул меу де адэпост.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Попоаре, ын орьче време, ынкредеци-вэ ын Ел, вэрсаци-вэ инимиле ынаинтя Луй! Думнезеу есте адэпостул ностру.
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Да, о нимика сунт фиий омулуй! Минчунэ сунт фиий оаменилор! Пушь ын кумпэнэ тоць лаолалтэ, ар фи май ушорь декыт о суфларе.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Ну вэ ынкредець ын асуприре ши ну вэ пунець нэдеждя задарникэ ын рэпире; кынд креск богэцииле, ну вэ липиць инима де еле!
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
О датэ а ворбит Думнезеу, де доуэ орь ам аузит кэ „путеря есте а луй Думнезеу.”
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
А Та, Доамне, есте ши бунэтатя, кэч Ту рэсплэтешть фиекэруя дупэ фаптеле луй.

< Masalimo 62 >