< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Para o músico chefe. Para Jeduthun. Um Salmo de David. Minha alma repousa somente em Deus. Minha salvação é dele.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Só ele é meu rochedo, minha salvação e minha fortaleza. Nunca serei muito abalado.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
How por muito tempo você vai agredir um homem? Todos vocês o jogariam no chão, como um muro inclinado, como uma cerca que se abana?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Eles pretendem atirá-lo de seu lugar elevado. Eles se deliciam com as mentiras. Eles abençoam com sua boca, mas amaldiçoam interiormente. (Selah)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Minha alma, espera em silêncio somente por Deus, pois minha expectativa é dele.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Só ele é meu rochedo e minha salvação, minha fortaleza. Eu não serei abalado.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Minha salvação e minha honra estão com Deus. A rocha da minha força, e meu refúgio, está em Deus.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Trust nele em todos os momentos, seu povo. Despeje seu coração diante dele. Deus é um refúgio para nós. (Selah)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Surely Os homens de baixo grau são apenas um sopro, e homens de alto grau são uma mentira. Nos balanços eles irão subir. Eles estão juntos mais leves que um sopro.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Don não confia na opressão. Não se torne vaidoso em roubos. Se as riquezas aumentam, não se preocupe com eles.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
God já falou uma vez; duas vezes ouvi isso, que o poder pertence a Deus.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
Também a ti, Senhor, pertence a bondade amorosa, para você recompensar cada homem de acordo com seu trabalho.

< Masalimo 62 >