< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
برای رهبر سرایندگان. برای یِدوتون. مزمور داوود. در سکوت برای خدا انتظار می‌کشم، زیرا نجات من از جانب اوست.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
او نجات دهنده و تنها صخرهٔ پناهگاه من است؛ او قلعهٔ محافظ من است، پس هرگز شکست نخواهم خورد.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
ای آدمیان، تا به کی بر من هجوم می‌آورید تا مرا که همچون دیواری فرو ریخته‌ام از پای درآورید؟
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
تنها فکرتان این است که مرا از این مقامی که دارم به زیر اندازید؛ شما دروغ را دوست دارید. با زبان خود مرا برکت می‌دهید اما در دلتان لعنتم می‌کنید.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
ای جان من، تنها نزد خدا آرام یاب، زیرا امید من بر اوست.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
او نجات دهنده و تنها صخرهٔ پناهگاه من است؛ او قلعهٔ محافظ من است، پس هرگز شکست نخواهم خورد.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
نجات و عزت من از جانب خداست؛ قوت و پناهگاه من خداست.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
ای مردم، همه وقت بر او توکل نمایید؛ غم دل خود را به او بگویید، زیرا خدا پناهگاه ماست.
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
همهٔ انسانها در مقابل او ناچیزند؛ اشخاص سرشناس و افراد بی‌نام و نشان، همگی در ترازوی او بالا می‌روند، زیرا از باد هم سبکترند.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
بر خشونت تکیه نکنید و به کسب ثروت از راه دزدی دل خوش نکنید، و هرگاه ثروتتان زیاد شود دل بر آن نبندید.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
شنیده‌ام که خدا بارها فرموده است که قوت از آن اوست،
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
اما بیش از آن شنیده‌ام که محبت نیز از آن اوست. خداوندا، تو هر کس را بر اساس کارهایش پاداش خواهی داد.

< Masalimo 62 >