< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
برای یدوتون سالار مغنیان. مزمور داود جان من فقط برای خدا خاموش می شود زیرا که نجات من از جانب اوست.۱
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
او تنها صخره و نجات من است و قلعه بلند من. پس بسیار جنبش نخواهم خورد.۲
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
تا به کی بر مردی هجوم می‌آورید تا همگی شما او راهلاک کنید مثل دیوار خمشده و حصار جنبش خورده؟۳
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
در این فقط مشورت می‌کنند که او را ازمرتبه‌اش بیندازند. و دروغ را دوست می‌دارند. به زبان خود برکت می‌دهند و در دل خود لعنت می‌کنند، سلاه.۴
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
‌ای جان من فقط برای خدا خاموش شو زیراکه امید من از وی است.۵
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
او تنها صخره و نجات من است و قلعه بلند من تا جنبش نخورم.۶
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
برخداست نجات و جلال من. صخره قوت من وپناه من در خداست.۷
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
‌ای قوم همه وقت بر اوتوکل کنید و دلهای خود را به حضور وی بریزید. زیرا خدا ملجای ماست، سلاه.۸
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
البته بنی آدم بطالت‌اند و بنی بشر دروغ. در ترازو بالا می‌روندزیرا جمیع از بطالت سبکترند.۹
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
بر ظلم توکل مکنید و بر غارت مغرور مشوید. چون دولت افزوده شود دل در آن مبندید.۱۰
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
خدا یک بارگفته است و دو بار این را شنیده‌ام که قوت از آن خداست.۱۱
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
‌ای خداوند رحمت نیز از آن تواست، زیرا به هر کس موافق عملش جزا خواهی داد.۱۲

< Masalimo 62 >