< Masalimo 62 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
I Andrianañahare avao ty fitamà’ ty fiaiko am-pitsiñañe, boak’ ama’e ty fandrombahañe ahy.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Ie avao ro lamilamiko naho ty fandrombahañe ahy; i haboam-pipalirakoy; tsy hasiotsiotse iraho.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Pak’ombia ty ho boroboñafe’ areo t’indaty? Hanjevoa’areo iaby hoe t’ie rindriñe mitondritse, ndra kijoly migavengaveñe.
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Ty hamotsahañe aze ami’ty haabo’e avao ro fikililia’ iareo: mpitea volam-bande; mitata am-palie, f’ie mamatse añ’ova ao Selà
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
I Andrianañahare avao ty liñisa’o ampitsiñañe, ty fiaiko toy; boak’ ama’e ty fisalalàko.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Ie avao ro lamilamiko naho fandrombahañe ahy; ty kijoliko abo; tsy hasiotse iraho.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
I Andrianañahare ty ampipohañe ty fandrombahañe ahy, naho ty engeko; ty lamilamin-kaozarako; fipalirako t’i Andrianañahare.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Miatoa ama’e nainai’e, ondatio, adoaño añatrefa’e ty arofo’ areo; fitsolohan-tika t’i Andrianañahare. Selà
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Toe hakoahañe avao o ana’ i Dameo, lañitse o ana’ ondatio; ie atraok’ am-pilanjàñe eo, le maivañe te ami’ty kofòke.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Ko iatoa’o ty fikatramoañe, naho ko manao fañirian-kafoake am-pikamerañe. Ndra te mionjoñe o varao ko ampirampian’ arofo.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Nitsara indraike t’i Andrianañahare, tsinanoko indroe ty hoe: An’Andrianañahare o haozarañeo,
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
vaho ama’o, ry Talè, ty fiferenaiñañe, songa tambeze’o mañeva o fitoloña’eo t’i ondaty.