< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
A karmesternek. Jedútún számára. Zsoltár Dávidtól. Bizony, Isten iránt légy csendben, lelkem; tőle van a segítségem.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Bizony, ő a sziklám és segítségem, mentsváram: nem tántorodom nagyot.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Meddig rohantok egy férfira — gyilkolnátok őt mindnyájan, – mint egy dűlő falra, betaszított kerítésre?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Bizony, fenségéről őt letaszítani határozták, hazugságot kedvelnek: kiki szájával áldanak, de belsejükben átkoznak. Széla.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Bizony, Istenre csendben várj, lelkem, mert tőle van reményem.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Bizony, ő a sziklám és segítségem, mentsváram: nem tántorodom.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Istennél van üdvöm és dicsőségem, erős sziklám, menedékem Istenben van.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Bízzatok benne minden időben, oh nép, öntsétek ki előtte szíveteket; Isten menedék nékünk! Széla.
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Bizony, lehelet az ember fiai, hazugság a férfi fiai; felkerülvén a mérlegre, ők leheletnél könnyebbek egyaránt.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Ne bízzatok a zsarolásban s rablottal ne hivalkodjatok; vagyon midőn virul, szívet ne fordítsatok rá.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Egyet beszélt Isten, kettő az, mit hallottam: hogy Istené az erő.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
És tied, Uram, a szeretet, te fizetsz kinek-hinek cselekedete szerint.

< Masalimo 62 >