< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
OIAIO, ke hilinai nei ko'u uhane i ke Akua; Nona mai no hoi ke ola no'u.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Oia wale no ko'u pohaku a me kuu ola; Oia ko'u wahi e malu ai, aole au e nauweuwe nui.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Pehea la ka loihi o ko oukou kukakuka hewa ku e i ke kanaka? E lukuia auanei oukou a pau, Me he pa hina la, me ka pa haalulu.
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Oiaio, ua ohumu lakou e kiola iho ia ia mai kona pono iho; Hauoli lakou i ka wahahee; Hoomaikai hoi lakou me ko lakou waha, Aka, maloko, ua hoino wale lakou. (Sila)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
E kuu uhane, e hilinai aku oe i ke Akua wale no; No ka mea, nona mai ka'u mea e kali nei.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Oia wale no ko'u pohaku a me kuu ola; Oia hoi ko'u wahi e malu ai, aole au e kulanalana.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Iloko o ke Akua ko'u ola a me ko'u nani: O ko'u pohaku paa, a o ko'u wahi malu, aia no i ke Akua.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
E hilinai aku ia ia i na manawa a pau, e na kanaka; E ninini aku i ko oukou naau imua ona: O ke Akua kahi e malu ai no kakou. (Sila)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Oiaio, he mea lapuwale na makaainana, He mea oiaio ole na kanaka koikoi; Aia waihoia ma ka mea kaupaona, Pau pu lakou i ka mama, aole ka ha.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Mai noho a hilinai i ka hooluhihewa ana: Mai noho a laua lapuwale ko oukou manao ma ka lawe wale ana. I ka wa e mahuahua ai ka waiwai, mai paulele ko oukou naau ilaila.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Hookahi olelo ana a ke Akua; Elua ko'u hoolohe ana i keia, no ke Akua ka mana.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
Nou no hoi, e ka Haku, e aloha mai; No ka mea, ua uku mai oe i kela kanaka i keia kanaka, e like me kana hana.

< Masalimo 62 >