< Masalimo 62 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Mon âme se repose en Dieu seul; c'est de lui que vient mon salut.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Lui seul est mon rocher, ma délivrance, ma haute retraite; je ne serai pas beaucoup ébranlé.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Jusques à quand vous jetterez-vous sur un homme, pour le détruire tous ensemble, comme un mur qui penche, comme une clôture ébranlée?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Ils ne font que consulter pour le faire tomber de son élévation; ils se plaisent au mensonge; de leur bouche ils bénissent, mais dans leur cœur ils maudissent. (Sélah)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Mon âme, repose-toi sur Dieu seul, car mon attente est en lui.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Lui seul est mon rocher, ma délivrance et ma haute retraite; je ne serai point ébranlé.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
En Dieu est mon salut et ma gloire; mon fort rocher, mon refuge est en Dieu.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Peuples, confiez-vous en lui en tout temps; répandez votre cœur devant lui; Dieu est notre retraite. (Sélah)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Les petits ne sont que néant; les grands ne sont que mensonge; placés dans la balance, ils seraient tous ensemble plus légers que le néant même.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Ne vous confiez pas dans la violence, et ne soyez pas séduits par la rapine; si les richesses abondent, n'y mettez pas votre cœur.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Dieu a parlé une fois, et je l'ai entendu deux fois: c'est que la force appartient à Dieu.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
A toi aussi, Seigneur, la miséricorde! Oui, tu rendras à chacun selon son œuvre.