< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Pour le chef musicien. A Jeduthun. Un psaume de David. Mon âme repose en Dieu seul. Mon salut vient de lui.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Lui seul est mon rocher, mon salut et ma forteresse. Je ne serai jamais fortement ébranlé.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Combien de temps allez-vous agresser un homme? Vous voulez tous le jeter à terre, comme un mur penché, comme une clôture chancelante?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Ils ont bien l'intention de le jeter à bas de sa position élevée. Ils se délectent de mensonges. Ils bénissent de la bouche, mais ils maudissent intérieurement. (Selah)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Mon âme, attends en silence Dieu seul, car c'est de lui que je m'attends.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Lui seul est mon rocher, mon salut, ma forteresse. Je ne serai pas ébranlé.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Mon salut et mon honneur sont auprès de Dieu. Le rocher de ma force, et mon refuge, est en Dieu.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Ayez confiance en lui en tout temps, vous autres. Répandez votre cœur devant lui. Dieu est un refuge pour nous. (Selah)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Les hommes de peu de valeur ne sont qu'un souffle, et les hommes de haut rang sont un mensonge. Dans les soldes, ils vont augmenter. Ils sont ensemble plus légers qu'un souffle.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Ne vous fiez pas à l'oppression. Ne devenez pas vaniteux dans le vol. Si les richesses augmentent, n'y attachez pas votre cœur.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Dieu a parlé une fois; J'ai entendu cela deux fois, ce pouvoir appartient à Dieu.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
A toi aussi, Seigneur, appartient la bonté, car tu récompenses chaque homme selon son travail.

< Masalimo 62 >