< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
To the victorie on Iditum, the salm of Dauid. Whether my soule schal not be suget to God; for myn heelthe is of hym.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
For whi he is bothe my God, and myn heelthe; my `taker vp, Y schal no more be moued.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Hou longe fallen ye on a man? alle ye sleen; as to a wal bowid, and a wal of stoon with out morter cast doun.
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Netheles thei thouyten to putte awei my prijs, Y ran in thirst; with her mouth thei blessiden, and in her herte thei cursiden.
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Netheles, my soule, be thou suget to God; for my pacience is of hym.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
For he is my God, and my saueour; myn helpere, Y schal not passe out.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Myn helthe, and my glorie is in God; God is the yyuer of myn help, and myn hope is in God.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Al the gaderyng togidere of the puple, hope ye in God, schede ye out youre hertis bifore hym; God is oure helpere with outen ende.
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Netheles the sones of men ben veyne; the sones of men ben liers in balauncis, that thei disseyue of vanytee in to the same thing.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Nile ye haue hope in wickidnesse, and nyle ye coueyte raueyns; if ritchessis be plenteuouse, nyle ye sette the herte therto.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
God spak onys, Y herde these twei thingis, that power is of God, and, thou Lord, mercy is to thee;
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
for thou schalt yelde to ech man bi hise werkis.

< Masalimo 62 >