< Masalimo 62 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
For the chief musician; after the manner of Jeduthun. A psalm of David. I wait in silence for God alone; my salvation comes from him.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
He alone is my rock and my salvation; he is my high tower; I will not be greatly moved.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
How long, all of you, will you attack a man, that you may tip him over like a leaning wall or a shaky fence?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
They consult with him only to bring him down from his honorable position; they love to tell lies; they bless him with their mouths, but in their hearts they curse him. (Selah)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
I wait in silence for God alone; for my hope is set on him.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
He alone is my rock and my salvation; he is my high tower; I will not be moved.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
With God is my salvation and my glory; the rock of my strength and my refuge are in God.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Trust in him at all times, you people; pour out your heart before him; God is a refuge for us. (Selah)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Surely men of low standing are vanity, and men of high standing are a lie; they will weigh lightly in the scales; weighed together, they are lighter than nothing.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Do not trust in oppression or robbery; and do not hope uselessly in riches, for they will bear no fruit; do not fix your heart on them.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
God has spoken once, twice have I heard this: power belongs to God.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
Also to you, Lord, belongs covenant faithfulness, for you pay back every person for what he has done.