< Masalimo 62 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Jeduthun aka mawt ham David kah Tingtoenglung Pathen dong bueng ah ka hinglu loh duemnah a khueh tih kai kah khangnah khaw amah taeng lamkah ni.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Amah te ka lungpang neh kai ham khangnah, ka imsang la om pai tih, ka thuen tlaih mahpawh.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Hlang te me hil nim na phom uh ve? Nangmih boeih loh aka ngooi pangbueng neh aka bung vongtung bangla na sah uh aya?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Anih te hmuensang lamloh heh ham rhep caai uh tih laithae a ngaingaih uh. A ka neh uem uh cakhaw a kotak ah a tap uh. (Selah)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Ka ngaiuepnah amah taeng lamkah halo dongah ka hinglu loh Pathen dong bueng ah ni a duem.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Anih bueng ni ka lungpang neh kai ham khangnah imsang la om tih ka tuen mahpawh.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
Pathen dongah kai kah khangnah, ka thangpomnah, ka sarhi lungpang om tih Pathen dongah ka hlipyingnah ni.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Pilnam loh a tue boeih khuiah BOEIPA dongah hangdang uh. Na thinko te amah hmai ah kingling lah. Pathen he mamih ham hlipyingnah ni. (Selah)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Tedae hlang capa rhoek he a honghi ni. Tongpa capa rhoek khaw laithae ni. Cooi dongah a honghi boeih lakah amih te yanghoep la a phoh.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Hnaemtaeknah dongah pangtung boel lamtah huencannah nen khaw hoemdawk boeh. A khuehtawn loh thaihsu cakhaw lungbuei pael boeh.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Pathen loh vai a thui te Pathen taengkah sarhi ni tila voeihnih ka yaak.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
Hlang te a khoboe bangla na thuung dongah sitlohnah tah ka Boeipa namah kah ni.