< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
За първия певец, по Едутуна. Давидов псалом. Душата ми тихо уповава само на Бога, От Когото е избавлението ми.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Само Той е канара моя и избавление мое, И прибежище мое; няма много да се поклатя.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
До кога, всички вие, ще нападате човека За да го съборите като наведена стена и разклатен плет?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Съветват се само да го тласкат от висотата му; Обичат лъжата; С устата си благославят, а в сърцето си кълнат. (Села)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Но ти, о душе моя, тихо уповавай само на Бога, Защото от Него очаквам помощ.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Само Той е канара моя, и избавление мое, И прибежище мое; няма да се поклатя.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
У Бога е избавлението ми и славата ми; Моята силна канара и прибежището ми е в Бога.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Уповавайте на Него, люде, на всяко време, Изливайте сърцата си пред Него; Бог е нам прибежище. (Села)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Наистина ниско поставените човеци са лъх, а високопоставените лъжа. Турени на везни те се издигат нагоре; Те всички са по-леки от суетата.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Не уповавайте на насилие, И не се надявайте суетно на грабителство; Богатство ако изникне, не прилепявайте към него сърцето си.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Едно нещо каза Бог, да! две неща чух, - Че силата принадлежи на Бога,
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
И че на Тебе, Господи, принадлежи и милостта; Защото Ти даваш на всекиго според делото му.

< Masalimo 62 >