< Masalimo 61 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
En Psalm Davids, till att föresjunga på strängaspel. Hör, Gud, mitt rop, och akta uppå mina bön.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Härnedre på jordene ropar jag till dig, när mitt hjerta i ångest är: För mig dock uppå en hög klippo.
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
Ty du äst min tillflykt; ett starkt torn för mina fiendar.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Jag vill bo uti dine hyddo till evig tid, och min tröst hafva under dina vingar. (Sela)
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
Ty du, Gud, hörer mina löften; du lönar dem väl, som ditt Namn frukta.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
Du gifver Konungenom långt lif, att hans år vara ifrå slägte till slägte;
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
Att han må evigliga för Gudi sittandes blifva. Bevisa honom godhet och trohet, att de bevara honom;
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Så vill jag lofsjunga dino Namne evinnerliga, att jag må betala mina löften dageliga.

< Masalimo 61 >