< Masalimo 61 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
Para el director del coro. Acompañado de instrumentos de cuerda. Un salmo de David. Por favor, Dios, escucha mi ruego de ayuda. Escucha mi oración.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Desde la distancia y lejos de mi hogar, clamo a ti a medida que mi fe desmaya. Llévame a la roca, en lo alto, donde pueda estar seguro,
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
porque tú eres mi protección, una torre fuerte en la que mis enemigos no pueden atacarme.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Déjame vivir contigoj por siempre y protégeme bajo la seguridad de tus alas. (Selah)
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
Porque tú, oh Dios, has escuchado las promesas que hice. A los que te aman tu carácter les has dado tu bendición especial.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
Por favor dale al rey muchos años más, y que su reino perdure a través de las generaciones.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
Que siempre viva en tu presencia. Que tu fidelidad y amor incondicional lo protejan.
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Entonces cantaré eternamente alabanzas a ti, y cada día cumpliré mi promesa hacia ti.

< Masalimo 61 >