< Masalimo 61 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
В конец, в песнех, Давиду Псалом. Услыши, Боже, моление мое, вонми молитве моей:
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
от конец земли к Тебе воззвах, внегда уны сердце мое: на камень вознесл мя еси, наставил мя еси,
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
яко был еси упование мое, столп крепости от лица вражия.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Вселюся в селении Твоем во веки, покрыюся в крове крил Твоих.
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
Яко Ты, Боже, услышал еси молитвы моя, дал еси достояние боящымся имене Твоего.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
Дни на дни царевы приложиши, лета его до дне рода и рода.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
Пребудет в век пред Богом: милость и истину его кто взыщет?
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Тако воспою имени Твоему во веки, воздати ми молитвы моя день от дне.