< Masalimo 61 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
Ki te tino kaiwhakatangi. Nekina. Na Rawiri. Whakarongo, e te Atua, ki taku karanga: tahuri mai ki taku inoi.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Ka karanga ahau ki a koe i te pito o te whenua, ina pehia toku ngakau: arahina ahau ki te kohatu e tiketike ake ana i ahau.
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
He piringa hoki koe moku: he pa kaha i te hoariri.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
Ka noho ahau ki tou tapenakara ake ake, ka okioki ki ou pakau hei piringa. (Hera)
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
Kua rongo nei hoki koe, e te Atua, i aku kupu tauranga kua homai e koe te wahi o te hunga e wehi ana ki tou ingoa.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
Ka whakaraneatia e koe nga ra o te kingi; ona tau ki nga whakatupuranga katoa.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
E noho ia i te aroaro o te Atua ake ake: whakaritea mai he aroha, he pono, hei tiaki i a ia.
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Penei ka himene ahau ki tou ingoa ake ake: ka whakamana e ahau aku kupu taurangi i tenei ra, i tenei ra.