< Masalimo 61 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
[For the Chief Musician. For a stringed instrument. By David.] Hear my cry, God. Listen to my prayer.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
From the most remote place of the earth, I will call to you, when my heart is overwhelmed. Lead me to the rock that is higher than I.
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
For you have been a refuge for me, a strong tower from the enemy.
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
I will dwell in your tent forever. I will take refuge in the shelter of your wings. (Selah)
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
For you, God, have heard my vows. You have given me the heritage of those who fear your name.
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
You will prolong the king's life; his years shall be for generations.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
He shall be enthroned in God's presence forever. Appoint your loving kindness and truth, that they may preserve him.
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
So I will sing praise to your name forever, that I may fulfill my vows day after day.

< Masalimo 61 >