< Masalimo 61 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe. Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu; mvetserani pemphero langa.
Til Sangmesteren. Til Strengespil. Af David.
2 Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka; tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.
Hør, o Gud, paa mit Raab og lyt til min Bøn!
3 Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga, nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.
Fra Jordens Ende raaber jeg til dig. Naar mit Hjerte vansmægter, løft mig da op paa en Klippe,
4 Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.
led mig, thi du er min Tilflugt, et mægtigt Taarn til Værn imod Fjenden.
5 Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga; mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.
Lad mig evigt bo som Gæst i dit Telt, finde Tilflugt i dine Vingers Skjul! (Sela)
6 Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu, zaka zake kwa mibado yochuluka.
Ja du, o Gud, har hørt mine Løfter, opfyldt deres Ønsker, der frygter dit Navn.
7 Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya; ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.
Til Kongens Dage lægger du Dage, hans Aar skal være fra Slægt til Slægt.
8 Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.
Han skal trone evigt for Guds Aasyn; send Naade og Sandhed til at bevare ham! Da vil jeg evigt love dit Navn og saaledes Dag efter Dag indfri mine Løfter.