< Masalimo 6 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
En Psalm Davids, till att föresjunga på åtta stränger. Ack! Herre, straffa mig icke i dina vrede, och näps mig icke i dine grymhet.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Herre, var mig nådelig, ty jag är svag; hela mig, Herre, ty mine ben äro förskräckte;
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
Och min själ är svårliga förskräckt; ack! Herre, huru länge?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Vänd dig, Herre, och undsätt mina själ; hjelp mig för dina mildhets skull.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
Ty i döden tänker man intet på dig; ho vill tacka dig i helvete? (Sheol )
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
Jag är så trött af suckande; jag gör mina säng flytande i hela nattene, och väter mitt lägre med mina tårar.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mitt ansigte är förfallet af sorg, och är gammalt vordet; ty jag varder trängd på alla sidor.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Viker ifrå mig, alle ogerningsmän; ty Herren hörer min gråt.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
Herren hörer mina bön; mina bön anammar Herren.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
Alle mine fiender komme på skam, och förskräckes svårliga; vände sig tillbaka, och komme på skam hasteliga.