< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
Senhor, não me reprehendas na tua ira, nem me castigues no teu furor.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Tem misericordia de mim, Senhor, porque sou fraco: sara-me, Senhor, porque os meus ossos estão perturbados.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
Até a minha alma está perturbada; mas tu, Senhor, até quando?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Volta-te, Senhor, livra a minha alma: salva-me por tua benignidade.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
Porque na morte não ha lembrança de ti; no sepulchro quem te louvará? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
Já estou cançado do meu gemido, toda a noite faço nadar a minha cama; molho o meu leito com as minhas lagrimas.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Já os meus olhos estão consumidos pela magoa, e teem-se envelhecido por causa de todos os meus inimigos.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Apartae-vos de mim todos os que obraes a iniquidade; porque o Senhor já ouviu a voz do meu pranto.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
O Senhor já ouviu a minha supplica; o Senhor acceitará a minha oração.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
Envergonhem-se e perturbem-se todos os meus inimigos; tornem atraz e envergonhem-se n'um momento.

< Masalimo 6 >