< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
Pour la fin, dans les cantiques, psaume de David, pour l’octave. Seigneur, ne me reprenez pas dans votre fureur, et ne me châtiez pas dans votre colère.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Ayez pitié de moi, Seigneur, parce que je suis infirme; guérissez-moi, Seigneur, parce que mes os sont ébranlés.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
Et mon âme est troublée à l’excès; mais vous, Seigneur, jusqu’à quand?…
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Revenez, Seigneur, et délivrez mon âme; sauvez-moi à cause de votre miséricorde.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
Parce que nul dans la mort ne se souvient de vous: et dans l’enfer qui vous glorifiera? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
Je me suis fatigué dans mon gémissement; je laverai chaque nuit mon lit de mes pleurs; j’arroserai ma couche de mes larmes.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mon œil a été troublé par l’indignation; j’ai vieilli au milieu de tous mes ennemis.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Retirez-vous de moi, vous tous qui opérez l’iniquité; parce que le Seigneur a exaucé la voix de mon pleur.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
Le Seigneur a exaucé ma supplication, le Seigneur a accueilli ma prière.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
Qu’ils rougissent et qu’ils soient remplis de trouble, tous mes ennemis; qu’ils s’en retournent très promptement et qu’ils rougissent.

< Masalimo 6 >