< Masalimo 6 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
Éternel, ne me reprends pas dans ton indignation, et ne me châtie pas dans ta colère.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Aie pitié de moi, Éternel! car je suis sans force; Éternel, guéris-moi, car mes os sont tremblants.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
Mon âme aussi est fort troublée; et toi, Éternel, jusques à quand?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Reviens, Éternel, délivre mon âme; sauve-moi pour l'amour de ta bonté!
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
Car dans la mort on ne se souvient point de toi; qui te célébrera dans le Sépulcre? (Sheol )
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
Je m'épuise à gémir; chaque nuit je baigne ma couche de pleurs, je trempe mon lit de mes larmes.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mon visage est tout défait de chagrin; il dépérit à cause de tous mes ennemis.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Éloignez-vous de moi, vous tous, ouvriers d'iniquité! Car l'Éternel a entendu la voix de mes pleurs.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
L'Éternel a entendu ma supplication, l'Éternel reçoit ma prière.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
Tous mes ennemis seront confus et saisis d'effroi; ils reculeront, ils seront soudain couverts de honte.