< Masalimo 6 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
For the Chief Musician; on stringed instruments, upon the eight-stringed lyre. A Psalm by David. LORD, don’t rebuke me in your anger, neither discipline me in your wrath.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Have mercy on me, LORD, for I am faint. LORD, heal me, for my bones are troubled.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
My soul is also in great anguish. But you, LORD—how long?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Return, LORD. Deliver my soul, and save me for your loving kindness’ sake.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
For in death there is no memory of you. In Sheol, who shall give you thanks? (Sheol )
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I am weary with my groaning. Every night I flood my bed. I drench my couch with my tears.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
My eye wastes away because of grief. It grows old because of all my adversaries.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Depart from me, all you workers of iniquity, for the LORD has heard the voice of my weeping.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
The LORD has heard my supplication. The LORD accepts my prayer.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
May all my enemies be ashamed and dismayed. They shall turn back, they shall be disgraced suddenly.