< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
To the choirmaster with stringed instruments on the sheminith a psalm of David. O Yahweh may not in anger your you rebuke me and may not in wrath your you discipline me.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Show favor to me O Yahweh for [am] frail I heal me O Yahweh for they are disturbed bones my.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
And self my it is disturbed exceedingly (and you *Q(K)*) O Yahweh until when?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Return! O Yahweh rescue! life my save me on account of covenant loyalty your.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
For there not in death [is] remembrance of you in Sheol who? will he give thanks to you. (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I have become weary - by groaning my I make swim in every night bed my with tear[s] my couch my I melt.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
It has wasted away from grief eye my it has grown weak with all opposers my.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Turn away from me O all [those who] do wickedness for he has heard Yahweh [the] sound of weeping my.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
He has heard Yahweh supplication my Yahweh prayer my he will accept.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
May they be ashamed - and they may be disturbed exceedingly all enemies my they will turn back they will be ashamed a moment.

< Masalimo 6 >