< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
“For the leader of the music; to be accompanied with stringed instruments; to the octave. A psalm of David.” O LORD! rebuke me not in thine anger; Chasten me not in thy hot displeasure!
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Have pity upon me, O LORD! for I am weak; Heal me, O LORD! for my bones tremble!
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
My soul, also, is sore troubled; And thou, O LORD! how long—?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Return, O LORD! and deliver me; Oh, save me according to thy mercy!
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
For in death no praise is given to thee; In the underworld who can give thee thanks? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I am weary with my groaning; All the night I make my bed to swim, And drench my couch with my tears.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mine eye is wasted with grief; It hath become old because of all my enemies.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Depart from me, all ye that do iniquity; For the LORD heareth the voice of my weeping.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
The LORD heareth my supplication; The LORD accepteth my prayer.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
All my enemies shall be ashamed and utterly confounded; They shall be turned back, and put to shame suddenly.

< Masalimo 6 >