< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
To him that excelleth on Neginoth upon the eith tune. A Psalme of Dauid. O lord, rebuke me not in thine anger, neither chastise me in thy wrath.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Haue mercie vpon me, O Lord, for I am weake: O Lord heale me, for my bones are vexed.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
My soule is also sore troubled: but Lord how long wilt thou delay?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Returne, O Lord: deliuer my soule: saue me for thy mercies sake.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
For in death there is no remembrance of thee: in the graue who shall prayse thee? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I fainted in my mourning: I cause my bed euery night to swimme, and water my couch with my teares.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mine eye is dimmed for despight, and sunke in because of all mine enemies.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Away from mee all ye workers of iniquitie: for the Lord hath heard the voyce of my weeping.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
The Lord hath heard my petition: the Lord will receiue my prayer.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
All mine enemies shall be confounded and sore vexed: they shall be turned backe, and put to shame suddenly.

< Masalimo 6 >