< Masalimo 6 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
To the chief Musician. On stringed instruments, upon Sheminith. A Psalm of David. Jehovah, rebuke me not in thine anger, and chasten me not in thy hot displeasure.
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Be gracious unto me, Jehovah, for I am withered; Jehovah, heal me, for my bones tremble.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
And my soul trembleth exceedingly: and thou, Jehovah, till how long?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Return, Jehovah, free my soul; save me for thy loving-kindness' sake.
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
For in death there is no remembrance of thee; in Sheol who shall give thanks unto thee? (Sheol h7585)
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
I am wearied with my groaning; all the night make I my bed to swim; I dissolve my couch with my tears.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mine eye wasteth away through grief; it hath grown old because of all mine oppressors.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Depart from me, all ye workers of iniquity; for Jehovah hath heard the voice of my weeping.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
Jehovah hath heard my supplication; Jehovah receiveth my prayer.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
All mine enemies shall be ashamed and tremble exceedingly; they will turn, they will be ashamed suddenly.

< Masalimo 6 >