< Masalimo 6 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
Til Sangmesteren; med Strengeleg; til Skeminith; en Psalme af David. O Herre! straf mig ikke i din Vrede og tugt mig ikke i din Harme!
2 Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
Herre! vær mig naadig, thi jeg er skrøbelig; læg mig, Herre! thi mine Ben skælve.
3 Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
Og min Sjæl skælver saare: Men du, Herre! — hvor længe?
4 Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Vend om, Herre! fri min Sjæl, frels mig for din Miskundheds Skyld!
5 Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol )
Thi der er ingen Ihukommelse af dig i Døden; hvo vil takke dig i Dødsriget? (Sheol )
6 Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
Jeg er træt af mit Suk, jeg væder min Seng den ganske Nat; jeg gennembløder mit Leje med min Graad.
7 Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
Mit Øje er hentæret af Sorg; det er blevet gammelt for alle mine Fjenders Skyld.
8 Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
Viger fra mig, alle I, som gøre Uret! thi Herren har hørt min Graads Røst.
9 Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
Herren har hørt min ydmyge Begæring, Herren vil antage min Bøn.
10 Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.
Alle mine Fjender skulle blive til Skamme og skælve saare; de skulle vige tilbage, de skulle blive til Skamme i et Øjeblik.