< Masalimo 59 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
Til sangmesteren; "Forderv ikke"; av David; en gyllen sang, da Saul sendte folk som tok vare på huset for å drepe ham. Fri mig fra mine fiender, min Gud, vern mig mot dem som reiser sig imot mig,
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
fri mig fra dem som gjør urett, og frels mig fra blodgjerrige menn!
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
For se, de lurer på mitt liv; sterke menn slår sig sammen imot mig, uten misgjerning og uten synd hos mig, Herre!
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Uten brøde hos mig stormer de frem og stiller sig op; våkn op for å møte mig, og se til!
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Ja du, Herre, hærskarenes Gud, Israels Gud, våkn op for å hjemsøke alle hedninger, vær ikke nådig imot nogen av de troløse nidinger! (Sela)
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
De kommer igjen om aftenen, tuter som hunder og løper rundt omkring i byen.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Se, det går en strøm av ord ut av deres munn; der er sverd på deres leber; for hvem hører det?
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
Men du, Herre, le, av dem, du spotter alle hedninger.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
Mot hans makt vil jeg bie på dig; for Gud er min borg.
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
Min Gud vil komme mig i møte med sin miskunnhet, Gud vil la mig se med lyst på mine fiender.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
Slå dem ikke ihjel, forat mitt folk ikke skal glemme det! La dem drive ustadig omkring ved din makt og styrt dem ned, du, vårt skjold, Herre!
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
Hvert ord på deres leber er en synd i deres munn; la dem så fanges i sitt overmot og for den forbannelses og løgns skyld som de fører i sin munn!
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
Gjør ende på dem i vrede, gjør ende på dem, så de ikke mere er til, og la dem vite at Gud er den som hersker i Jakob inntil jordens ender! (Sela)
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
Og de kommer igjen om aftenen, tuter som hunder og løper rundt omkring i byen.
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
De farer omkring efter mat; om de ikke blir mette, blir de således natten over.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
Men jeg vil synge om din styrke, og jeg vil juble om morgenen over din miskunnhet; for du er min borg og min tilflukt den dag jeg er i nød.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
Min styrke! For dig vil jeg synge; for Gud er min borg, min miskunnhets Gud.